Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 14:50-57 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

50. naphe mbalame imodzi m'mbale yadothi, pamwamba pa madzi oyenda;

51. natenge mtengo wamkungudza ndi hisope, ndi ubweya wofiira, ndi mbalame yamoyo, nazibviike m'mwazi wa mbalame yakuphayo, ndi m'madzi oyenda, nawaze kasanu ndi kawiri m'nyumba;

52. nayeretsenyumbandi mwazi wa mbalame, ndi madzi oyenda, ndi mbalame yamoyo, ndi mtengo wamkungudza, ndi hisope, ndi ubweya wofiira.

53. Koma ataye mbalame yamoyo kunja kwa mudzi kuthengo koyera; motero aicitire coitetezera nyumbayo; ndipo idzakhala yoyera.

54. Ici ndi cilamulo ca nthenda iri yonse yakhate, ndi yamfundu;

55. ndi ya khate la cobvala, ndi la nyumba;

56. ndi yacotupa, ndi yankhanambo, ndi yacikanga;

57. kulangiza tsiku loti cikhala codetsa, ndi tsiku loti cikhala coyera; ici ndi cilamulo ca khate.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 14