Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 14:35-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. pamenepo mwini nyumbayo adzauze wansembe, kuti, Ndiyesa muli ngati nthenda m'nyumba.

36. Ndipo wansembe aziuza kuti aturutse zonse za m'nyumba, asanalowe kudzaona nthendayi, zinthu zonse ziri m'nyumba zingakhale zodetsedwa; ndipo atatero wansembe alowe kukaona nyumbayi;

37. naone nthendayo, ndipo taonani, nthenda ikakhala yosumbudzuka m'makoma a nyumba yobiriwira kapena yofiira, ndipo maonekedwe ace yakumba kubzola khoma;

38. pamenepo wansembe azituruka ku khomo la nyumba, natseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri;

39. ndipo wansembe abwerenso tsiku lacisanu ndi ciwiri, naonenso, ndipo taonani, ngati nthenda yakula m'makoma a nyumba;

40. pamenepo wansembe auze kuti agumule miyalayi pali nthenda, naitayire ku malo akuda kunja kwa mudzi;

41. napalitse nyumba m'kati monsemo, natayire ku malo akuda kunja kwa mudzi dothi adapalako;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 14