Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 14:23-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo tsiku lacisanu ndi citatu abwere nao kwa wansembe, ku khomo la cihema cokomanako, pamaso pa Yehova.

24. Ndipo wansembe atenge mwana wa nkhosa wa nsembe yoparamula, ndi muyeso wa mafuta, ndipo wansembe aziweyule nsembe yoweyula pamaso pa Yehova;

25. naphe mwana wa nkhosa wa nsembe yoparamula, ndipo wansembe atengeko mwazi wa nsembe yoparamula, naupake pa ndewerere ya khutu la ku dzanja lamanja la iye akuti ayeretsedwe, ndi pa cala cacikuru ca dzanja lace lamanja, ndi pa cala cacikuru ca phazi lace la ku dzanja lamanja;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 14