Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 13:37-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Koma monga momwe apenyera iye, ngati mfundu yaima pomwe, ndipo pamera tsitsi lakuda, mfundu yapola, ndiye woyera, ndipo wansembe amuche woyera.

38. Ndipo ngati mwamuna kapena mkazi ali ndi zikanga pa khungu la thupi lace, zikanga zoyerayera;

39. wansembe aziona; ndipo taonani ngati zikanga ziri pa khungu la thupi lao zikhala zotuwatuwa; ndilo thuza labuka pakhungu; ndiye woyera.

40. Ndipo ngati tsitsi la munthu lathothoka, ndiye wadazi; koma woyera.

41. Ndipo ngati tsitsi lathothoka pamphumi pace ndiye wa masweswe, koma woyera.

42. Koma ngati pali nthenda yotuuluka pakati pa dazi lace la pamutu, kapena la pamphumi, ndipo khate lirikubuka pakati pa dazi lace la pamutu, kapena la pamphumi.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 13