Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 11:11-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. inde muziyese zonyansa; musamadya nyama zao; mitembo yao zikunyansireni.

12. Ziri zonse zopanda zipsepse kapena mamba m'madzimo muziyese zonyansa.

13. Ndipo mwa mbalame muziziyesa zonyansa izi; siziyenera kuzidya, zonyansa ndi izi: mphungu, ndi nkhwazi, ndi cikambi;

14. ndi muimba, ndi mphamba mwa mtundu wace;

15. kungubwi mwa mtundu wace;

16. ndi nthiwatiwa, ndi cipudo, ndi kakoa, ndi kabawi mwa mtundu wace;

17. ndi nkhutunkhutu ndi nswankhono ndi mancici;

18. tsekwe, bvuwo, ndi dembu;

19. indwa, ndi cimeza monga mwa mtundu wace, ndi sadzu, ndi mleme.

20. Zokwawa zonse zakuuluka zokhala ndi miyendo inai, muziyesa izi zonyansa,

Werengani mutu wathunthu Levitiko 11