Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 4:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Anthu anga aonongeka cifukwa ca kusadziwa; popeza unakana kudziwa, Inenso ndikukaniza, kuti usakhale wansembe wanga; popeza waiwala cilamulo ca Mulungu wako, Inenso ndidzaiwala ana ako.

7. Monga anacuruka, momwemo anandicimwira; ndidzasanduliza ulemerero wao ukhale manyazi.

8. Adyerera cimo la anthu anga, nakhumbira cosalungama cao, yense ndi mtima wace.

9. Ndipo kudzakhala monga anthu, momwemo wansembe; ndipo ndidzawalanga cifukwa canjira zao, ndi kuwabwezera macitidwe ao.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 4