15. Cinkana iwe, Israyeli, ucita citole, koma asaparamule Yuda; ndipo musafika inu ku Giligala, kapena kukwera ku Betaveni, kapena kulumbira, Pali Yehova.
16. Pakuti Israyeli wacita kuuma khosi ngati ng'ombe yaikazi yaing'ono youma khosi; tsopano Yehova adzawadyetsa ngati mwana wa nkhosa ku thengo lalikuru.
17. Efraimu waphatikana ndi mafano, mlekeni.
18. Cakumwa cao casasa, acita citole kosalekeza; akuru ao akonda manyazi kwambiri.
19. Mphepo yamkulunga m'mapiko ace, ndipo adzacita manyazi cifukwa ca nsembe zao.