Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 12:6-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. M'mwemo utembenukire kwa Mulungu wako, sunga cifundo ndi ciweruzo, nuyembekezere Mulungu wako kosalekeza.

7. Ndiye Mkanani, m'dzanja lace muli miyeso yonyenga, akonda kusautsa.

8. Ndipo Efraimu anati, Zedi ndasanduka wolemera, ndadzionera cuma m'nchito zonse ndinazigwira; sadzapeza mwa ine mphulupulu yokhala cimo.

9. Koma Ine ndine Yehova Mulungu wako cicokere dziko la Aigupto, ndidzakukhalitsanso m'mahema, monga masiku a masonkhano oikika.

10. Ndalankhulanso ndi aneneri, ndipo Ine ndacurukitsa masomphenya; ndi pa dzanja la aneneri ndinanena ndi mafanizo.

11. Kodi Gileadi ndiye wopanda pace? akhala acabe konse; m'Giligala aphera nsembe yang'ombe; inde maguwa ao a nsembe akunga miulu yamiyala m'micera ya munda.

12. Ndipo Yakobo anathawira ku thengo la Aramu, ndi Israyeli anagwira nchito cifukwa ca mkazi, ndi cifukwa ca mkazi anaweta nkhosa.

13. Ndipo mwa mneneri Yehova anakweretsa Israyeli kucokera m'Aigupto, ndi mwa mneneri anasungika.

14. Efraimu wautsa mkwiyo wowawa, m'mwemo Iye adzamsiyira mwazi wace, ndi Ambuye wace adzambwezera comtonza cace.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 12