Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 11:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamene Israyeli anali mwana, ndinamkonda, ndinaitana mwana wanga ali m'Aigupto.

2. Monga anawaitana, momwemo anawacokera; anaphera nsembe Abaala, nafukizira mafano osema.

3. Koma Ine ndinaphunzitsa Efraimu kuyenda, ndinawafungata m'manja mwanga; koma sanadziwa kuti ndinawaciritsa.

4. Ndinawakoka ndi zingwe za munthu, ndi zomangira za cikondi; ndinakhala nao ngati iwo akukweza goli pampuno pao, ndipo ndinawaikira cakudya.

5. Iye sadzabwerera kumka ku dziko la Aigupto, koma Asuri adzakhala mfumu yace, popeza anakana kubwera.

6. Ndi lupanga lidzagwera midzi yace, lidzatha mipiringidzo yace, ndi kuononga cifukwa ca uphungu wao.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 11