Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hagai 2:10-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Tsiku la makumi awiri ndi anai la mwezi wacisanu ndi cinai, caka caciwiri ca Dariyo, mau a Yehova anadza mwa Hagai mneneri, ndi kuti,

11. Atero Yehova wa makamu: Funsatu ansembe za cilamulo, ndi kuti,

12. Munthu akanyamulira nyama yopatulika m'ngudulira, nakhudza mkate, kapena ndiwo, kapena vinyo, kapena mafuta, kapena cakudya ciri conse, ndi ngudulira, kodi cisandulika copatulika? Ndipo ansembe anayankha nati, Iai.

13. Pamenepo Hagai anati, Munthu wodetsedwa ndi mtembo akakhudza kanthu ka izi, kodi kali kodetsedwa kanthuka? Ndipo ansembe anayankha nati, Kadzakhala kodetsedwa.

14. Ndipo Hagai anayankha, nati, Momwemo anthu awa, ndi momwemo mtundu uwu pamaso panga, ati Yehova; ndi momwemo nchito iri yonse ya manja ao; ndi ici acipereka, ciri codetsedwa.

15. Ndipo tsono, samalirani, kuyambira lero ndi m'tsogolomo, kuti, kusanaikidwe mwala pa mwala m'Kacisi wa Yehova,

16. pamenepo ponse munthu akadza ku mulu woyenera miyeso makumi awiri, pali khumi yokha; munthu akadza ku coponderamo mphesa kudzatunga mbiya makumi asanu, pali makumi awiri okha.

17. Ndinakukanthani ndi cinsikwi ndi cinoni ndi matalala m'nchito zonse za manja anu, koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.

18. Musamalire, kuyambira lero ndi m'tsogolo, kuyambira tsiku la makumi awiri ndi cinai la mwezi wacisanu ndi cinai, kuyambira tsiku lija anamanga maziko a Kacisi wa Yehova, samalirani.

Werengani mutu wathunthu Hagai 2