Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hagai 2:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku la makumi awiri ndi cimodzi la mweziwo, mau a Yehova anadza mwa Hagai mneneri, ndi kuti,

2. Unenetu kwa Zerubabele, mwana wa Sealitiyeli, ciwanga ca Yuda, ndi kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkuru wa ansembe, ndi kwa otsala a anthu, kuti,

3. Adatsala ndani mwa inu amene anaona nyumba iyi m'ulemerero wace woyamba? ndipo muiona yotani tsopano? Kodi siikhala m'maso mwanu ngati cabe?

4. Koma limbika tsopano, Zerubabele, ati Yehova; ulimbikenso Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkuru wa ansembe; ndipo mulimbike inu nonse anthu a m'dziko, ati Yehova, ndi kucita; pakui. Ine ndiri pamodzi ndi inu, ati Yehova wa makamu;

5. monga momwe ndinapangana nanu muja munaturuka m'Aigupto, ndi Mzimu wanga unakhala pakati pa inu; musamaopa inu.

6. Pakuti atero Yehova wa makamu: Kamodzinso, katsala kanthawi, ndidzagwedeza miyamba ndi dziko lapansi, ndi nyanja, ndi mtunda womwe;

7. ndipo ndidzagwedeza amitundu onse, ndi zofunika za amitundu onse zidzafika, ndipo ndidzadzaza nyumba iyi ndi ulemerero, ati Yehova wa makamu.

8. Siliva ndi wanga, golidi ndi wanga, ati Yehova wa makamu.

9. Ulemerero wotsiriza wa nyumba iyi udzaposa woyambawo, ati Yehova wa makamu; ndipo m'malo muno ndidzapatsa mtendere, ati Yehova wa makamu.

Werengani mutu wathunthu Hagai 2