Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hagai 1:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Cifukwa cace tsono, atero Yehova wa makamu: Mtima wanu usamalire njira zanu.

6. Mwabzala zambiri, koma mututa pang'ono; mukudya, koma osakhuta; mukumwa, koma osakoledwa; mudzibveka, koma palibe wofundidwa; ndi iye wolembedwa nchito yakulipidwa alandirira kulipirako m'thumba lobooka.

7. Atero Yehova wa makamu: Mtima wanu usamalire njira zanu.

8. Kwerani ku dziko la mapiri, ndi kukwera nayo mitengo, nimumange nyumbayi; ndipo kudzandikomera, ndipo ndidzalemekezedwa, ati Yehova.

9. Munayembekezera zambiri, koma taonani, pang'ono; ndipo, mutabwera napo kwanu, ndinauzirapo. Cifukwa ninji? ati Yehova wa makamu. Cifukwa ca nyumba yanga yokhala yopasuka, ndipo nuthamangira yense kunyumba kwace.

10. M'mwemo cifukwa ca inu kumwamba kukaniza mame, ndi nthaka ikaniza zipatso zace.

Werengani mutu wathunthu Hagai 1