Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hagai 1:3-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pamenepo mau a Yehova anadza mwa Hagai mneneri, ndi kuti,

4. Kodi imeneyi ndiyo nthawi yakuti inu nokha mukhala m'nyumba zanu zocingidwa m'katimo, ndi nyumba iyi ikhale yopasuka?

5. Cifukwa cace tsono, atero Yehova wa makamu: Mtima wanu usamalire njira zanu.

6. Mwabzala zambiri, koma mututa pang'ono; mukudya, koma osakhuta; mukumwa, koma osakoledwa; mudzibveka, koma palibe wofundidwa; ndi iye wolembedwa nchito yakulipidwa alandirira kulipirako m'thumba lobooka.

7. Atero Yehova wa makamu: Mtima wanu usamalire njira zanu.

8. Kwerani ku dziko la mapiri, ndi kukwera nayo mitengo, nimumange nyumbayi; ndipo kudzandikomera, ndipo ndidzalemekezedwa, ati Yehova.

9. Munayembekezera zambiri, koma taonani, pang'ono; ndipo, mutabwera napo kwanu, ndinauzirapo. Cifukwa ninji? ati Yehova wa makamu. Cifukwa ca nyumba yanga yokhala yopasuka, ndipo nuthamangira yense kunyumba kwace.

10. M'mwemo cifukwa ca inu kumwamba kukaniza mame, ndi nthaka ikaniza zipatso zace.

11. Ndipo ndinaitana cirala cidzere dziko, ndi mapiri, ndi tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta, ndi zimene ibala nthaka, ndi anthu, ndi zoweta, ndi nchito zonse za manja.

12. Pamenepo Zerubabele mwana wa Sealitiyeli, ndi Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkuru wa ansembe, ndi otsala onse a anthu, anamvera mau a Yehova Mulungu wao, ndi mau a Hagai mneneri, monga Yehova Mulungu wao adamtuma; ndipo anthu anaopa pamaso pa Yehova.

Werengani mutu wathunthu Hagai 1