Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Habakuku 2:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Tsoka iye wakupindulitsira nyumba yace phindu loipa, kuti aike cisanja cace ponyamuka, kuti alanditsidwe m'dzanja la coipa!

10. Wapangira nyumba yako camanyazi, pakuononga mitundu yambiri ya anthu, ndipo wacimwira moyo wako.

11. Pakuti mwala wa m'khoma upfuula, ndi mtanda wa kuphaso udzaubvomereza.

12. Tsoka tye wakumanga mudzindi mwazi, nakhazikitsa mudzi ndi cisalungamo!

13. Taonani, sicicokera kwa Yehova wa makamu kodi kuti mitundu ya anthu ingogwirira moto nchito, ndi anthu angodzilemetsa pa zopanda pace?

14. Pakuti dziko lapansi lidzadzazidwa ndi cidziwitso ca ulemerero wa Yehova, monga madzi aphimba pansi panyanja.

Werengani mutu wathunthu Habakuku 2