Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Habakuku 1:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Penyani mwa amitundu, penyetsetsani, nimudabwe kwakukuru, pakuti ndicita nchito masiku anu, imene simudzabvomera cinkana akufotokozerani.

6. Pakuti taonani, ndiukitsa Akasidi, mtundu uja wowawa ndi waliwiro, wopitira, pa citando ca dziko lapansi, kulowa m'malo mosati mwao, mukhale mwao mwao.

7. Ali oopsa, acititsa mantha, ciweruzo cao ndi ukulu wao zituruka kwa iwo eni.

8. Akavalo ao aposa anyalugwe liwiro lao, aposa mimbulu ya madzulo ukali wao, ndipo apakavalo ao atanda; inde apakavalo ao afumira kutali; auluka ngati ciombankhanga cofulumira kudya.

9. Adzera ciwawa onsewo; nkhope zao zikhazikika zolunjika m'tsogolo; asonkhanitsa andende ngati mcenga,

Werengani mutu wathunthu Habakuku 1