Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 7:11-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Caka ca mazana asanu ndi limodzi ca moyo wa Nowa, mwezi waciwiri, tsiku la khumi ndi asanu ndi awiri la mwezi, tsiku lomwelo akasupe onse a madzi akuru anasefuka, ndi mazenera a kumwamba anatseguka.

12. Ndipo mvula inali pa dziko lapansi masiku makumi anai usana ndi usiku.

13. Tsiku lomwelo analowa m'cingalawamo Nowa, ndi Semu, ndi Hamu, ndi Yafeti, ana a Nowa, ndi mkazi wace wa Nowa, ndi akazi atatu a ana ace pamodzi nao:

Werengani mutu wathunthu Genesis 7