Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 5:6-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo Seti anakhala ndi moyo zaka zana kudza zisanu, nabala Enosi;

7. ndipo Seti anakhala ndi moyo, atabala Enosi, zaka mazana asanu ndi atatu kudza zisanu ndi ziwiri: ndipo anabala ana amuna ndi akazi:

8. masiku ace onse a Seti anali zaka mazana asanu ndi anai kudza khumi ndi ziwiri; ndipo anamwalira.

9. Ndipo Enosi anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi anai, nabala Kenani;

10. ndipo anakhala ndi moyo Enosi, atabala Kenani, zaka mazana asanu ndi atatu kudza khumi ndi zisanu: ndipo anabala ana amuna ndi akazi.

11. Masiku ace onse a Enosi anali mazana asanu ndi anai kudza zisanu; ndipo anamwalira.

12. Ndipo Kenani anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi awiri, ndipo anabala Mahalalele:

13. ndipo Kenani anakhala ndi moyo, atabala Mahalalele zaka mazana asanu ndi atatu kudza makumi anai, ndipo anabala ana amuna ndi akazi;

14. masiku ace onse a Kenani anali zaka mazana asanu ndi anai kudza khumi; ndipo anamwalira.

15. Ndipo Mahalalele anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi limodzi kudza zisanu, nabala Yaredi;

16. ndipo Mahalalele anakhala ndi moyo, atabala Yaredi, zaka mazana asanu ndi atatu kudza makumi atatu, nabala ana amuna ndi akazi:

17. masiku ace onse a Mahalalele anali zaka mazana asanu ndi atatu kudza makumi asanu ndi anai ndi zisanu; ndipo anamwalira.

18. Ndipo Yaredi anakhala ndi moyo zaka zana kudza makumi asanu ndi limodzi ndi ziwiri, nabala Enoke;

19. ndipo Yaredi anakhala ndi moyo, atabala Enoke, zaka mazana asanu ndi atatu, nabala ana amuna ndi akazi;

20. masiku ace onse a Yaledi anali zaka mazana asanu ndi anai kudza maitumi asanu ndi limodzi ndi ziwiri: ndipo anamwalira.

Werengani mutu wathunthu Genesis 5