Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 5:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo Adamu anakhala ndi moyo zaka zana limodzi kudza makumi atatu, nabala mwana wamwamuna m'cifanizo cace; namucha dzina lace Seti.

4. Masiku ace Adamu atabala Seti, anali zaka mazana asanu ndi atatu; ndipo anabala ana amuna ndi akazi.

5. Masiku ace onse anakhala ndi moyo Adamu anali zaka mazana asanu ndi anai, kudza makumi atatu; ndipo anamwalira.

6. Ndipo Seti anakhala ndi moyo zaka zana kudza zisanu, nabala Enosi;

7. ndipo Seti anakhala ndi moyo, atabala Enosi, zaka mazana asanu ndi atatu kudza zisanu ndi ziwiri: ndipo anabala ana amuna ndi akazi:

8. masiku ace onse a Seti anali zaka mazana asanu ndi anai kudza khumi ndi ziwiri; ndipo anamwalira.

9. Ndipo Enosi anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi anai, nabala Kenani;

Werengani mutu wathunthu Genesis 5