16. ndipo Mahalalele anakhala ndi moyo, atabala Yaredi, zaka mazana asanu ndi atatu kudza makumi atatu, nabala ana amuna ndi akazi:
17. masiku ace onse a Mahalalele anali zaka mazana asanu ndi atatu kudza makumi asanu ndi anai ndi zisanu; ndipo anamwalira.
18. Ndipo Yaredi anakhala ndi moyo zaka zana kudza makumi asanu ndi limodzi ndi ziwiri, nabala Enoke;
19. ndipo Yaredi anakhala ndi moyo, atabala Enoke, zaka mazana asanu ndi atatu, nabala ana amuna ndi akazi;
20. masiku ace onse a Yaledi anali zaka mazana asanu ndi anai kudza maitumi asanu ndi limodzi ndi ziwiri: ndipo anamwalira.