Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 5:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ili ndi buku la mibadwo ya Adamu. Tsiku lomwe Mulungu analenga munthu anamlenga m'cifanizo ca Mulungu;

2. anawalenga iwo mwamuna ndi mkazi, nawadalitsa iwo nacha mtundu wao anthu, tsiku lomwe anawalenga iwo.

3. Ndipo Adamu anakhala ndi moyo zaka zana limodzi kudza makumi atatu, nabala mwana wamwamuna m'cifanizo cace; namucha dzina lace Seti.

4. Masiku ace Adamu atabala Seti, anali zaka mazana asanu ndi atatu; ndipo anabala ana amuna ndi akazi.

5. Masiku ace onse anakhala ndi moyo Adamu anali zaka mazana asanu ndi anai, kudza makumi atatu; ndipo anamwalira.

6. Ndipo Seti anakhala ndi moyo zaka zana kudza zisanu, nabala Enosi;

7. ndipo Seti anakhala ndi moyo, atabala Enosi, zaka mazana asanu ndi atatu kudza zisanu ndi ziwiri: ndipo anabala ana amuna ndi akazi:

8. masiku ace onse a Seti anali zaka mazana asanu ndi anai kudza khumi ndi ziwiri; ndipo anamwalira.

9. Ndipo Enosi anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi anai, nabala Kenani;

Werengani mutu wathunthu Genesis 5