Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 49:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Dani adzaweruza anthu ace,Monga limodzi la mafuko a Israyeli.

17. Dani adzakhala njoka m'khwalala,Songo panjira,Imene iluma zitende za kavalo,Kuti womkwera wace agwe cambuyo.

18. Ndadikira cipulumutso canu, Yehova.

19. Ndi Gadi, acifwamba adzampsinja iye;Koma iye adzapsinja pa citende cao.

20. Ndi Aseri, cakudya cace ndico mafuta,Ndipo adzapereka zolongosoka zacifumu.

Werengani mutu wathunthu Genesis 49