Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 49:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yakobo anaitana ana ace amuna, nati, Sonkhanani inu, kuti ndikuuzeni inu cimene cidzakugwerani inu masiku akudzawo.

2. Sonkhanani, tamvani, ana amuna a Yakobo:Tamverani Israyeli atate wanu:

3. Rubeni, ndiwe woyamba wanga, mphamvu yanga ndi ciyambi ca mphamvu yanga;Ulemu wopambana, ndi mphamvu yopambana.

4. Wobwabwada ngati madzi; sudzapambana;Cifukwa unakwera pa kama wa atate wako;Pamenepo unaipitsapo; anakwera paja ndigonapo.

5. Simeoni ndi Levi ndiwo abale;Zida za mphulupulu ndizo malupanga ao.

Werengani mutu wathunthu Genesis 49