Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 45:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo mudzafotokozera atate wanga za ulemerero wanga wonse m'Aigupto, ndi zonse mwaziona; ndipo muzifulumira ndi kutsitsira kuno atate wanga.

14. Ndipo anagwa pakhosi pace pa Benjamini, nalira; ndipo Benjamini nalira pakhosi pace.

15. Ndipo anampsompsona abale ace onse, nalilira iwo; ndipo pambuyo pace abale ace onse anaceza naye.

16. Ndipo mbiri yace inamveka m'nyumba ya Farao, kuti abale ace a Yosefe afika; ndipo inamkomera Farao, ndi anyamata ace.

17. Ndipo Farao anati kwa Yosefe, Nena ndi abale ako, Citani ici; senzetsani nyama zanu, ndi kupita kunka ku dziko la Kanani;

Werengani mutu wathunthu Genesis 45