Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 42:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Tumizani mmodzi wa inu akatenge, adze naye mphwanu: ndipo inu mudzamangidwa kuti mau anu ayesedwe, ngati zoona ziri mwa inu: penatu, pali moyo wa Farao, muli ozonda ndithu.

17. Ndipo anaika onse m'kaidi masiku atatu.

18. Ndipo Yosefe anati kwa iwo tsiku lacitatu, Citani ici, kuti mukhale ndi moyo; ine ndiopa Mulungu;

19. ngati muli oona, mmodzi wa abale anu amangidwe m'kaidi momwemo; mukani inu, mupite naye tirigu wa njala ya mabanja anu;

Werengani mutu wathunthu Genesis 42