Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 42:11-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Tonse tiri ana amuna a munthu mmodzi; tiri oona, akapolo anu, sitiri ozonda.

12. Ndipo iye anati kwa iwo, Iai, koma mwadzera kuti muone usiwa wa dziko.

13. Nati iwo, Akapolo anu ndife abale khumi, ana amuna a munthu mmodzi m'dziko la Kanani; ndipo, taonani, wamng'ono ali ndi atate wathu lero; ndipo palibe mmodzi.

14. Ndipo Yosefe anati kwa iwo, dico cimene ndinakunenani inu, kuti, Ndinu ozonda.

15. Mudzayesedwa ndi ici, pali moyo wa Farao, simudzaturuka muno, koma akadze kuno mphwanu ndiko.

16. Tumizani mmodzi wa inu akatenge, adze naye mphwanu: ndipo inu mudzamangidwa kuti mau anu ayesedwe, ngati zoona ziri mwa inu: penatu, pali moyo wa Farao, muli ozonda ndithu.

17. Ndipo anaika onse m'kaidi masiku atatu.

Werengani mutu wathunthu Genesis 42