Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 41:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. ndipo, taona, ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zina zinaturuka pambuyo pao zosauka ndi za maonekedwe oipa ndi zoonda, zoipa zotere sindinazione m'dziko la Aigupto;

20. ndipo ng'ombe zazikazi zoonda ndi za maonekedwe oipa zinadya ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zonenepa,

21. Ndipo pamene zinadya sizinadziwika kuti zinadya; koma zinaipabe m'maonekedwe ao monga poyamba.

22. Pamenepo ndinauka. Ndipo ndinaona m'kulota kwanga, taona, ngala zisanu ndi ziwiri zinamera pa mbuwa imodzi zodzala ndi zabwino;

Werengani mutu wathunthu Genesis 41