Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 4:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo Lameke anadzitengera yekha akazi awiri: dzina lace la wina ndi Ada, dzina lace la mnzace ndi Zila.

20. Ndipo Ada anabala Yabala; iye ndiye atate wao wa iwo okhala m'mahema, akuweta ng'ombe,

21. Ndi dzina la mphwace ndilo Yubala; iye ndiye atate wao wa iwo oyimba zeze ndi citoliro.

22. Ndipo Zila, iyenso anabala Tubala-Kaini, mwini wakuphunzitsa amisiri onse a mkuwa ndi a citsulo; mlongo wace wa Tubala-Kaini ndi Nama.

23. Lameke ndipo anati kwa akazi ace:Tamvani mau anga, Ada ndi Zila;Inu akazi a Lameke, mverani kunena kwanga:Ndapha munthu wakundilasa ine,Ndapha mnyamata wakundiphweteka ine,

Werengani mutu wathunthu Genesis 4