Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 39:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo ananena kwa iye monga mau awa, nati, Analowa kwa ine kapolo wa Cihebri uja, munabwera naye kwathu, kundipunza ine:

18. ndipo panali pamene ndinakweza mau anga ndi kupfuula, iye anasiya cobvala cace kwa ine, nathawira kunja.

19. Ndipo panali pamene mbuyace anamva mau a mkazi wace, amene ananena kwa iye, kuti, Coteroci anandicitira ine kapolo wako; kuti iye anapsya mtima.

20. Ndipo mbuyace wa Yosefe anamtenga iye namuika m'kaidi, umo anamangidwa akaidi a mfumu: ndipo iye anali m'mwemo m'kaidimo.

Werengani mutu wathunthu Genesis 39