Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 38:27-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndipo panali nthawi ya kubala kwace, taonani, amapasa anali m'mimba mwace.

28. Ndipo panali pamene anabala kuti mmodzi anaturutsa dzanja; ndipo namwino anatenga cingwe cofiira namanga pa dzanja lace, kuti, Uyu anayamba kubadwa.

29. Ndipo panali pamene iye ana bweza dzanja lace, kuti, taona, mbale wace anabadwa, ndipo namwino anati, Wadziposolera wekha bwanji? cifukwa cace dzina lace linachedwa Pereze.

30. Ndipo pambuyo pace anabadwa mbale wace, amene anali ndi cingwe cofiira pamkono pace, dzina lace linachedwa Zera.

Werengani mutu wathunthu Genesis 38