Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 38:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo panali nthawi yomweyo, kuti Yuda anatsikira kwa abale ace nalowa kwa M-adulami, dzina lace Hira.

2. Ndipo Yuda anaona kumeneko mwana wamkazi wa Mkanani dzina lace Sua: ndipo anamtenga, nalowa kwa iye.

3. Ndipo anatenga pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Eri.

4. Ndipo anatenganso pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Onani.

5. Ndipo anabalanso mwana wamwamuna, namucha dzina lace Sela: ndipo iye anali pa Kezibi pamene mkazi anambala iye,

6. Ndipo Yuda anamtengera Eri mwana wace woyamba mkazi, ndipo dzina lace ndilo Tamara.

Werengani mutu wathunthu Genesis 38