1. Ndipo panali nthawi yomweyo, kuti Yuda anatsikira kwa abale ace nalowa kwa M-adulami, dzina lace Hira.
2. Ndipo Yuda anaona kumeneko mwana wamkazi wa Mkanani dzina lace Sua: ndipo anamtenga, nalowa kwa iye.
3. Ndipo anatenga pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Eri.
4. Ndipo anatenganso pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Onani.