Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 37:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Koma Israyeli anamkonda Yosefe koposa ana ace onse, pakuti anali mwana wa ukalamba wace; ndipo anamsokera iye malaya amwinjiro.

4. Ndipo abale ace anaona kuti atate wace anamkonda iye koposa abale ace onse: ndipo anamuda iye, ndipo sanathe kulankhula ndi iye mwamtendere.

5. Yosefe ndipo analota loto, nawafotokozera abale ace; ndipo anamuda iye koposa.

6. Ndipo iye anati kwa iwo, Tamvanitu loto limene ndalota:

Werengani mutu wathunthu Genesis 37