Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 36:22-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndi ana a Lotani anali Hori ndi Hemamu: mlongo wace wa Lotani anali Timna.

23. Ana a Sobali ndi awa: Alivani ndi Manahati ndi Ebali, Sefo ndi Onamu.

24. Ana a Zibeoni ndi amenewa: Aia ndi Ana; ameneyo ndiye Ana uja anapeza akasupe a madzi amoto m'cipululu, pakudyetsa aburu a Zibeoni atate wace.

25. Ana a Ana ndi awa: Disoni ndi Oholibama mwana wamkazi wa Ana.

26. Ana a Disoni ndi awa: Hemadani ndi Esibani ndi Itirani, ndi Kerana.

27. Ana a Ezeri ndi awa: Biliha, ndi Zavani, ndi Akani.

28. Ana a Disoni ndi awa: Uzi ndi Arana.

29. Mafumu obadwa kwa Ahori: mfumu Lotani, mfumu Sobali, mfumu Zibeoni, mfumu Ana,

30. mfumu Disoni, mfumu Ezeri, mfumu Disani; amenewa ndi mafumu obadwa kwa Ahori, monga mwa maufumu ao m'dziko la Seiri.

31. Amenewo ndi mafumu analamulira m'dziko la Edomu, asadalamulire ana a Israyeli mfumu ali yense.

32. Ndipo Bela mwana wamwamuna wa Beori, analamulira m'Edomu, ndipo dzina la mudzi wace ndilo Dinaba.

Werengani mutu wathunthu Genesis 36