19. Amenewa ndi ana amuna a Esau, amenewa ndi mafumu ao; yemweyo ndi Edomu.
20. Amenewa ndi ana amuna a Seiri Mhori, okhala m'dzikomo: Lotani ndi Sobala, ndi Zibeoni, ndi Ana,
21. ndi Disoni ndi Ezeri ndi Disani; amenewa ndi mafumu obadwa kwa Ahori, ana a Seiri, m'dziko la Edomu.
22. Ndi ana a Lotani anali Hori ndi Hemamu: mlongo wace wa Lotani anali Timna.
23. Ana a Sobali ndi awa: Alivani ndi Manahati ndi Ebali, Sefo ndi Onamu.
24. Ana a Zibeoni ndi amenewa: Aia ndi Ana; ameneyo ndiye Ana uja anapeza akasupe a madzi amoto m'cipululu, pakudyetsa aburu a Zibeoni atate wace.
25. Ana a Ana ndi awa: Disoni ndi Oholibama mwana wamkazi wa Ana.