Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 35:8-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo anafa Debora mlezi wa Rebeka, naikidwa kunsi kwa Beteli, pansi pa mtengo wathundu; ndipo anacha dzina lace AlioniBakuti.

9. Ndipo Mulungu anamuonekeranso Yakobo, pamene iye anacokera m'Padanaramu, namdalitsa iye.

10. Ndipo Mulungu anati kwa iye, Dzina lako ndi Yakobo; dzina lako silidzachedwanso Yakobo, koma dzina lako lidzakhala Israyeli: ndipo anamucha dzina lace Israyeli.

11. Ndipo Mulungu anati kwa iye, Ine ndine Mulungu Wamphamvuyonse: ubale, ucuruke; mwa iwe mudzaturuka mtundu ndi gulu la mitundu, ndipo mafumu adzaturuka m'cuuno mwako;

12. ndipo dziko limene ndinapatsa kwa Abrahamu ndi kwa Isake ndidzalipatsa kwa iwe ndipo ndidzapatsa mbeu zako za pambuyo pako dzikoli.

13. Ndipo Mulungu anakwera kumcokera iye kumene ananena naye.

14. Ndipo Yakoboanaimiritsamwala pamalo pamene ananena ndi iye, coimiritsa camwala: ndipo anathira pamenepo nsembe yothira, nathirapo mafuta.

15. Ndipo anacha dzina lace la pamalo pamene Mulungu ananena ndi iye, Beteli.

16. Ndipo anacokera ku Beteli: ndipo panatsala nthawi asanafike ku Efrati: ndipo Rakele anabala nabvutidwa.

Werengani mutu wathunthu Genesis 35