Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 35:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. ana amuna a Biliha mdzakazi wace wa Rakele: ndiwo Dani ndi Nafitali;

26. ndipo ana amuna a Zilipa mdzakazi wace wa Leya: ndiwo Gadi ndi Aseri: amenewo ndi ana amuna a Yakobo amene anabala iye m'Padanaramu.

27. Ndipo Yakobo anafika kwa Isake atate wace ku Mamre, ku KiriyatiAriba (ndiwo Hebroni) kumene anakhala Abrahamu ndi Isake.

28. Ndipo masiku a Isake anali zaka zana limodzi kudza makumi asanu ndi atatu.

29. Ndipo Isake anatsirizika nafa, nasonkhanitsidwa kwa anthu a mtundu wace, wokalamba ndi wa masiku okwanira: ndipo Esau ndi Yakobo ana ace amuna anamuika iye.

Werengani mutu wathunthu Genesis 35