Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 35:22-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo panali pamene Israyeli anakhala m'dzikomo, Rubeni anamuka nagona ndi Biliha, mkazi wamng'ono wa atate wace: ndipo Israyeli anamva.Ana amuna a Yakobo anali khumi ndi awiri:

23. ana amuna a Leya: ndiwo Rubeni mwana woyamba wa Yakobo, ndi Simeoni ndi Levi, ndi Yuda, ndi Zebuloni, ndi Isakara;

24. ana amuna a Rakele: ndiwo Yosefe ndi Benjamini;

25. ana amuna a Biliha mdzakazi wace wa Rakele: ndiwo Dani ndi Nafitali;

26. ndipo ana amuna a Zilipa mdzakazi wace wa Leya: ndiwo Gadi ndi Aseri: amenewo ndi ana amuna a Yakobo amene anabala iye m'Padanaramu.

27. Ndipo Yakobo anafika kwa Isake atate wace ku Mamre, ku KiriyatiAriba (ndiwo Hebroni) kumene anakhala Abrahamu ndi Isake.

28. Ndipo masiku a Isake anali zaka zana limodzi kudza makumi asanu ndi atatu.

29. Ndipo Isake anatsirizika nafa, nasonkhanitsidwa kwa anthu a mtundu wace, wokalamba ndi wa masiku okwanira: ndipo Esau ndi Yakobo ana ace amuna anamuika iye.

Werengani mutu wathunthu Genesis 35