Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 35:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo pakutsirizika iye, pakuti anamwalira, anamucha dzina lace Benoni; koma atate wace anamucha Benjamini.

19. Ndipo anafa Rakele, naikidwa pa njira va ku Efrati (ndipo Betelehemu),

20. Ndipo Yakobo anaimiritsa mwala pamanda pace: umenewo ndi coimiritsa ca pa manda a Rakele kufikira lero.

21. Ndipo Israyeli anapita namanga hema wace patseri pa nsanja ya Edere.

22. Ndipo panali pamene Israyeli anakhala m'dzikomo, Rubeni anamuka nagona ndi Biliha, mkazi wamng'ono wa atate wace: ndipo Israyeli anamva.Ana amuna a Yakobo anali khumi ndi awiri:

23. ana amuna a Leya: ndiwo Rubeni mwana woyamba wa Yakobo, ndi Simeoni ndi Levi, ndi Yuda, ndi Zebuloni, ndi Isakara;

Werengani mutu wathunthu Genesis 35