Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 30:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo Biliha anatenga pakati, nambalira Yakobo mwana wamwamuna.

6. Rakele ndipo anati, Mulungu wandiweruzira ine, namva mau anga, nandipatsa ine mwana; cifukwa cace anamucha dzina lace Dani.

7. Ndipo Biliha mdzakazi wace wa Rakele anatenganso pakati, nambalira Yakobo mwana wamwamuna waciwiri.

8. Ndipo Rakele anati, Ndi malimbano a Mulungu ndalimbana naye mkuru wanga, ndipo ndapambana naye; ndipo anamucha dzina lace Nafitali.

Werengani mutu wathunthu Genesis 30