Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 30:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo Biliha anatenga pakati, nambalira Yakobo mwana wamwamuna.

6. Rakele ndipo anati, Mulungu wandiweruzira ine, namva mau anga, nandipatsa ine mwana; cifukwa cace anamucha dzina lace Dani.

7. Ndipo Biliha mdzakazi wace wa Rakele anatenganso pakati, nambalira Yakobo mwana wamwamuna waciwiri.

8. Ndipo Rakele anati, Ndi malimbano a Mulungu ndalimbana naye mkuru wanga, ndipo ndapambana naye; ndipo anamucha dzina lace Nafitali.

9. Pamene Leya anaona kuti analeka kubala, anatenga Zilipa mdzakazi wace, nampatsa iye kwa Yakobo kuti akhale mkazi wace.

10. Ndipo Zilipa mdzakazi wace wa Leya anambalira Yakobo mwana wamwamuna.

11. Ndipo Leyaanati, Wamwai ine! ndipo anamucha dzina lace Gadi.

12. Ndipo Zilipa mdzakazi wa Leya anambalira Yakobo mwana wamwamuna waciwiri.

Werengani mutu wathunthu Genesis 30