Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 30:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndipo panali pamene Rakele anabala Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, Undisudzule ine ndinke kwathu ku dziko langa.

26. Undipatse ine akazi anga ndi ana anga cifukwa ca iwowa ndakutumikira iwe, ndimuke: cifukwa udziwa iwe nchito imene ndinakugwirira iwe.

27. Ndipo Labani anati kwa iye, Ngatitu ndikapeza ufulu pamaso pako, ukhale, cifukwa ndazindikira kuti Yehova wandidalitsa ine cifukwa ca iwe.

28. Ndipo iye anati, Undipangire ine malipiro ako, ndipo ndidzakupatsa.

29. Ndipo iye anati kwa Labani, Udziwa iwe comwe ndakutumikira iwe ndi comwe zacita zoweta zako ndi ine.

Werengani mutu wathunthu Genesis 30