Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 30:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Pambuyo pace ndipo anabala mwana wamkazi, namucha dzina lace Dina.

22. Ndipo Mulungu anakumbukila Rakele, ndipo Mulungu anamvera iye, natsegula m'mimba mwace.

23. Ndipo anatenga pakati, nabala mwana wamwamuna, nati, Mulungu wacotsa manyazi anga;

24. namucha dzina lace Yosefe; ndipo anati, Yehova anandionjezera ine mwana wamwamuna wina.

25. Ndipo panali pamene Rakele anabala Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, Undisudzule ine ndinke kwathu ku dziko langa.

Werengani mutu wathunthu Genesis 30