Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 28:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Isake anamuitana Yakobo, namdalitsa iye, namuuza iye, nati kwa iye, Usatenge mkazi wa ana akazi a Kanani.

2. Tauka, nupite ku Padanaramu, ku nyumba ya Betuele, atate wa amai ako; ukadzitengere mkazi wa kumeneko kwa ana akazi a Labani mlongo wace wa amako.

3. Mulungu Wamphamvuyonse akudalitse iwe, akubalitse iwe, akucurukitse iwe, kuti ukhale khamu la anthu:

4. akupatse iwe mdalitso wa Abrahamu, iwe ndi mbeu zako pamodzi nawe: kuti ulowe m'dziko limene ukhalamo mlendo, limene Mulungu anampatsa Abrahamu.

5. Ndipo Isake anamlola Yakobo amuke, ndipo ananka ku Padanaramu kwa Labani, mwana wace wa Betuele Msuriya, mlongo wace wa Rebeka, amai wao wa Yakobo ndi Esau.

6. Ndipo anaona Esau kuti Isake anamdalitsa Yakobo namtumiza ku Padanaramu kuti atenge mkazi wa kumeneko;

Werengani mutu wathunthu Genesis 28