Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 27:3-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. tsopano tengatu zida zako ndi phodo lako ndi uta wako, numuke kuthengo kundisakira ine nyama;

4. nundikonzere ine cakudya cokolera conga comwe ndicikonda ine, nudze naco kwa ine kuti ndidzadye; kuti moyo wanga ukadalitse iwe ndisanafe.

5. Ndipo anamva Rebeka pamene Isake ananena ndi Esau mwana wace. Ndipo Esau ananka kuthengo kukasaka nyama ndi kubwera nayo.

6. Ndipo Rebeka ananena kwa Yakobo mwana wace, nati, Taona ndinamva atate wako alinkunena ndi Esau mkuru wako kuti,

7. Unditengere ine nyama, undikonzere ine cakudya cokolera, kuti ndidzadye, ndi kudalitsa iwe pamaso pa Yehova, ndisanafe.

8. Tsopanotu mwana wanga, tamvera mau anga monga momwe nditi ndikuuze iwe.

9. Pitatu kubusa, ukanditengere ine kumeneko tiana tiwiri tabwino ta mbuzi; ndikonzere nato cakudya cokolera ca atate wako conga comwe acikonda:

10. ndipo udzapita naco kwa atate wako, kuti adye, ndi kukudalitsa iwe asanafe,

11. Yakobo ndipo anati kwa Rebeka amace, Taonani, Esau mkuru wanga ndiye munthu waubweya, ine ndine munthu, wosalala.

12. Kapena atate wanga adzandiyambasa, ndipo ndidzaoneka pamaso pace ngati wakunyenga; pamenepo ndidzadzitengera ine temberero, si mdalitso.

13. Ndipo amace anati kwa iye, Pa ine likhale temberero lako mwana wanga; koma tamvera mau anga, kazimuka kunditengera timeneto.

14. Ndipo anamuka nakatenga nadza nato kwa amace; amace ndipo anakonza cakudya cokolera conga cimene anacikonda atate wace.

15. Ndipo Rebeka anatenga zobvala zokoma za Esau, mwana wace wamkuru zinali m'nyumba, nabveka nazo Yakobo mwana wace wamng'ono;

16. ndipo anabveka zikopa za tiana tambuzi pa manja ace ndi pakhosi pace posalala;

17. ndipo anapereka m'dzanja la mwana wace Yakobo cakudya cokoleraco, ndi mikate imene anaipanga.

18. Ndipo iye analowa kwa atate wace, nati, Atate wanga; iye anati, Ndine pano; ndani iwe mwana wanga?

19. Ndipo Yakobo anati kwa atate wace, Ndine Esau mwana wanu wamkuru; ndacita monga mwandiuza ine; ukanitu, khalani tsonga, idyani nyama yanga kuti moyo wanu undidalitse ine.

20. Ndipo Isake anati kwa mwana wace, Unaipeza msanga bwanji mwana wanga? Ndipo anati, Cifukwa kuti Yehova Mulungu wanu anandiyendetsa ine bwino.

21. Ndipo Isake anati kwa Yakobo, Sendera kuno, ndikuyambase mwana wanga, ngati ndiwe mwana wanga Esau ndithu, kapena wina.

Werengani mutu wathunthu Genesis 27