Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 26:31-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Ndipo analawira m'mamawa nalumbirirana wina ndi mnzace; ndipo Isake anawalola amuke, ndipo anauka kucokera kwa iye m'mtendere.

32. Ndipo panali tsiku lomwelo anyamata ace a Isake anadza namuuza iye za citsime cimene anakumba, nati kwa iye, Tapeza madzi.

33. Ndipo anacha dzina lace Seba, cifukwa cace dzina la mudziwo ndi Beereseba kufikira lero lino.

34. Pamene Esau anali wa zaka makumi anai, anakwatira Yuditi mwana wamkazi wa Beeri Mhiti, ndi Basemati mwana wamkazi wa Elone Mhiti:

35. ndipo iwo anapweteka mtima wa Isake ndi wa Rebeka.

Werengani mutu wathunthu Genesis 26