1. Ndipo Sara anali wa zaka zana limodzi kudza makumi awiri ndi zisanu ndi ziwiri: ndizo zaka za moyo wa Sara.
2. Ndipo Sara anafa m'Kiriyati-araba (ndiwo Hebroni), m'dziko la Kanani; ndipo Abrahamu anadza ku maliro a Sara, kuti amlire.
3. Ndipo Abrahamu anauka pa wakufa wace, nanena kwa ana a Heti, nati,
4. Ine ndine mlendo wakukhala ndi inu: mundipatse ndikhale ndi manda pamodzi ndi inu, kuti ndiike wakufa wanga ndisamthirenso maso.
5. Ndipo ana a Heti anayankha Abrahamu nati kwa iye,
6. Mutimvere ife mfumu, ndinu karonga wamkuru pakati pa ife; muike wakufa wanu m'manda mwathu mosankhika: palibe munthu yense wa ife adzakaniza manda ace, kuti muike wakufa wanu.
7. Ndipo anauka Abrahamu naweramira anthu a m'dzikomo, ana a Heti.
8. Ndipo ananena nao, kuti, Ngati mukandibvomereza kuti ndiike wakufa wanga ndisamthirenso maso, mundimvere ine, mundinenere ine kwa Efroni mwana wace wa Zohari,