Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 21:21-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo anakhala m'cipululu ca Parana; ndipo amace anamtengera iye mkazi wa ku dziko la Aigupto.

22. Ndipo panali nthawi yomweyo. Abimeleke ndi Fikolo kazembe wa nkhondo yace anati kwa Abrahamu, kuti, Mulungu ali pamodzi ndi iwe m'zonse uzicita iwe;

23. tsopano iwe undilumbirire ine pano pa Mulungu kuti sudzandinyenga ine, kapena mwana wanga, kapena mdzukulu wanga: koma monga ufulu ndakucitira iwe udzandicitire ine, ndi dziko lomwe wakhalamo, ngati mlendo.

24. Ndipo Abrahamu anati, Ine ndidzalumbira.

25. Ndipo Abrahamu anamdzudzula Abimeleke cifukwa ca citsime ca madzi, anyamata ace a Abimeleke anacilanda.

26. Ndipo anati Abimeleke, Sindinadziwe amene anacita ico; ndipo iwe sunandiuze ine, ndiponso sindinamve koma lero lino.

27. Ndipo Abrahamu anatenga nkhosa ndi ng'ombe, nampatsa Abimeleke, ndipo anapangana pangano onse awiriwo.

28. Ndipo Abrahamu anapatula ana a nkhosa akazi asanu ndi awiri pa okha.

29. Ndipo Abimeleke anati kwa Abrahamu, Nanga ana a nkhosa akazi asanu ndi awiri amene wapatula pa okha?

30. Ndipo anati, Ana a nkhosa akazi asanu ndi awiriwa uwalandire pa dzanja langa, kuti akhale mboni zanga, kuti ndakumba ine citsime cimeneci.

Werengani mutu wathunthu Genesis 21