Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 19:35-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Ndipo anamwetsa vinyo atate wao usiku womwenso; wamng'ono ndipo anauka nagona naye; ndipo iye sanadziwa pomwe anagona ndi pomwe anauka.

36. Ndipo ana akazi awiri a Loti anali ndi pakati pa atate wao.

37. Woyamba ndipo anabala mwana wamwamona, namcha dzina lace. Moabu; yemweyo ndi atate wa Amoabu kufikira lero.

38. Wamng'ono ndipo anabala mwana wamwamuna, namcha dzina lace Benammi; yemweyo ndi atate wa Aamoni kufikira lero.

Werengani mutu wathunthu Genesis 19