Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 19:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Koma mkazi wace anaceuka ali pambuyo pace pa Loti, nasanduka mwala wamcere.

27. Ndipo Abrahamu analawiram'mamawa kunka kumalo kumene anaima pamaso pa Yehova:

28. ndipo anayang'anira ku Sodomu ndi ku Gomora ndi ku dziko lonse la cigwa, ndipo anapenya, taonanitu, utsi wa dzikolo unakwera, monga utsi wa ng'anjo.

29. Ndipo panali pamene Mulungu anaononga midzi ya m'cigwa, Mulungu anakumbukira Abrahamu, naturutsa Loti pakati pa cionongeko, pamene anaononga midzi m'mene anakhalamo Loti.

Werengani mutu wathunthu Genesis 19