Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 19:25-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. ndipo anaononga midziyo, ndi cigwa conse, ndi onse akukhala m'midzimo, ndi zimene zimera panthaka.

26. Koma mkazi wace anaceuka ali pambuyo pace pa Loti, nasanduka mwala wamcere.

27. Ndipo Abrahamu analawiram'mamawa kunka kumalo kumene anaima pamaso pa Yehova:

28. ndipo anayang'anira ku Sodomu ndi ku Gomora ndi ku dziko lonse la cigwa, ndipo anapenya, taonanitu, utsi wa dzikolo unakwera, monga utsi wa ng'anjo.

29. Ndipo panali pamene Mulungu anaononga midzi ya m'cigwa, Mulungu anakumbukira Abrahamu, naturutsa Loti pakati pa cionongeko, pamene anaononga midzi m'mene anakhalamo Loti.

30. Ndipo Loti anabwera kuturuka m'Zoari nakhala m'phiri ndi ana akazi awiri pamodzi naye: cifukwa anaopa kukhala m'Zoari, ndipo anakhata m'phanga, iye ndi ana ace akazi.

Werengani mutu wathunthu Genesis 19